MOYO WATHU WACHIKHRISTU
Kukhulupirika Kumagwirizana ndi Zimene Timaganiza
Timasonyeza kuti ndife okhulupirika, osati chifukwa cha zochita kapena zolankhula zathu zokha, koma chifukwa cha zimenenso timaganiza. (Sl 19:14) N’chifukwa chake Baibulo limatilimbikitsa kuti tiziganizira zinthu zilizonse zoona, zofunika kwambiri, zolungama, zoyera, zachikondi, zoyamikirika, khalidwe labwino lililonse, ndi chilichonse chotamandika. (Afi 4:8) N’zoona kuti nthawi zina sitingapeweretu kuganiza zinthu zoipa. Komabe kudziletsa kungatithandize kuti tichotse maganizo oipawo n’kuyamba kuganizira zinthu zabwino. Kukhalabe okhulupirika pa zimene timaganiza kungatithandize kuti tizichita zinthu mokhulupirika.—Mko 7:21-23.
M’munsi mwa lemba lililonse, lembani maganizo amene muyenera kupewa: